26. Indetu ndinena ndi iwe, sudzaturukamo konse, koma utalipa kakobiri kakumariza ndiko.
27. Munamva kuti kunanenedwa, Usacite cigololo;
28. koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kucita naye cigololo mumtima mwace.
29. Koma 1 ngati diso lake lamanja likulakwitsa iwe, ulikolowole, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe, kuti cimodzi ca ziwalo zako cionongeke, losaponyedwa thupi lako lonse m'gehena.
30. Ndipo 2 ngati dzanja lako lamanja likulakwitsa iwe, ulidule, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe kuti cimodzi ca ziwalo zako cionongeke, losamuka thupi lako lonse kugehena.
31. Kunanenedwanso, Yense wakucotsa mkazi wace 3 ampatse iye cilekaniro:
32. koma Ine ndinena kwa inu, kuti 4 yense wakucotsa mkazi wace, kosati cifukwa ca cigololo, amcititsa cigololo: ndipo amene adzakwata wocotsedwayo acita cigololo.
33. Ndiponso, munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, 5 Usalumbire konama, koma udzapereka kwa Ambuye zolumbira zako:
34. koma Ine ndinena kwa inu, 6 Musalumbire konse, kapena kuchula Kumwamba, cifukwa kuli cimpando ca Mulungu;
35. 7 kapena kuchula dziko lapansi, cifukwa liri popondapo mapazi ace; kapena kuchula Yerusalemu, cifukwa kuli mzinda wa Mfumu yaikurukuru.
36. 8 Kapena usalumbire ku mutu wako, cifukwa sungathe kuliyeretsa mbu kapena kulidetsa bii tsitsi limodzi.
37. 9 Kama manenedwe anu akhale, Inde, inde; Iai, iai; ndipo coonjezedwa pa izo cicokera kwa woipayo.
38. Munamva kuti kunanenedwa, 10 Diso kulipa diso, ndi dzino kulipa dzino:
39. koma ndinena kwa inu, 11 Musakanize munthu woipa; koma amene adzakupanda iwe pa tsaya lako Lamanja, umtembenuzire linanso.