Mateyu 5:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo m'mene Iye anaona makamu, anakwera m'phiri; ndipo m'mene Iye anakhala pansi, anadza kwa Iye ophunzira ace;

2. ndipo anatsegula pakamwa, nawaphunzitsa iwo, nati:

3. Odala ali osauka mumzimu; cifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

4. Odala ali acisoni; cifukwa adzasangalatsidwa.

5. Odala ali akufatsa; cifukwa adzalandira dziko lapansi.

6. Odala ali akumva njala ndi ludzu la cilungamo; cifukwa adzakhuta.

7. Odala ali akucitira cifundo; cifukwa adzalandira cifundo.

8. Odala ali oyera mtima; cifukwa adzaona Mulungu.

Mateyu 5