2. nanena, Tembenukani mitima; cifukwa Ufumu wa Kumwamba wayandikira.
3. Pakuti uyu ndiye ananenayo Yesaya mneneri, kuti,Mau a wopfuula m'cipululu,Konzani khwalala la Ambuye,Lungamitsani njira zace.
4. Ndipo Yohane yekhayo anali naco cobvala cace ca ubweya wangamila, ndi lamba lacikopa m'cuuno mwace; ndi cakudya cace cinali dzombe ndi uci wa kuthengo.
5. Pamenepo panamturukira iye ku Yerusalemu, ndi Yudeya lonse, ndi dziko lonse loyandikana ndi Yordano;
6. nabatizidwa ndi iye mu mtsinjewo wa Yordano, alikuulula macimo ao.
7. Ndipo iye pakuona ambiri a Afarisi ndi a Asaduki akudza ku ubatizo wace, anati kwa iwo, Obadwa a njoka inu, ndani anakulangizani kuthawa mkwiyo ulinkudza?
8. Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:
9. ndipo musamayesa kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye Abrahamu; pakuti ndinena kwa inu kuti mwa miyala iyi Mulungu akhoza kuukitsira Abrahamu ana.
10. Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cifukwa cace mtengo uli wonse wosabala zipatso zabwino udulidwa nuponyedwa pamoto,