Mateyu 27:39-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo anthu akupitirirapo 1 anamcitira mwano Iye ndi kupukusa mitu yao,

40. nati, Nanga 2 Iwe, wopasula Kacisi, ndi kummanganso masiku atatu, tadzipulumutsa wekha; 3 ngati uli Mwana wa Mulungu, tatsika pamtandapo.

41. Comweconso ansembe akuru, pamodzi ndi alembi ndi akuru anamcitira cipongwe, nati,

42. Anapulumutsa ena, sangathe kudzipulumutsa yekha. Ndiye Mfumu ya Ayuda; atsike tsopano pamtandapo, ndipo tidzamkhulupirira Iye.

43. 4 Amakhulupirira Mulungu; Iye ampulumutse tsopano, ngati amfuna; pakuti anati, Ine ndine Mwana wa Mulungu.

44. Ndiponso 5 acifwambawo opacikidwa pamodzi ndi Iye, anamlalatira Iye mau amodzimodzi.

45. Ndipo 6 ora lacisanu ndi cimodzi panali mdima pa dziko lonse, kufikira ora lacisanu ndi cinai.

46. Ndipo poyandikira ora lacisanu ndi cinai, Yesu 7 anapfuula ndi mau akuru, kunena, Eli, Eli, lama sabakitani? ndiko kunena kuti, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?

47. Ndipo ena a iwo akuimirira komweko, pamene anamva, ananena, Uyo aitana Eliya.

48. Ndipo pomwepa mmodzi wa iwo anathamanga, 8 natenga cinkhupule, nacidzaza ndi vinyo wosasa, naciika pabango, namwetsa Iye.

49. Koma ena anati, Taleka, tione ngati Eliya adzafika kudzampulumutsa.

50. Ndipo Yesu, 9 pamene anapfuula ndi mau akuru, anapereka mzimu wace.

51. Ndipo onani, 10 cinsaru cocinga ca m'Kacisi cinang'ambika pakati, kucokera kumwamba kufikira pansi; ndipo dziko linagwedezeka, ndi miyala inang'ambika;

Mateyu 27