Mateyu 27:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pakudza mamawa, ansembe akuru ndi akuru a anthu onse anakhala upo wakumcitira Yesu, kuti amuphe;

2. ndipo anammanga Iye, namuka naye, nampereka Iye kwa Pilato kazembeyo.

3. Pamenepo Yudase yemwe anampereka Iye, poona kuti Iye anatsutsidwa kuti afe, analapa, nabweza ndalama zija zasiliva makumi atatu kwa ansembe akuru ndi akuru,

4. nanena, Ndinacita koipa ine, pakupereka mwazi wosalakwa. Koma iwo anati, Tiri naco ciani ife? udzionere wekha.

Mateyu 27