Mateyu 26:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali pamene Yesu anatha mau onse amenewa, anati kwa ophunzira ace,

2. Mudziwa kuti akapita masiku awiri, Paskha ufika, ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kupacikidwa pamtanda.

3. Pomwepo anasonkhana ansembe akuru, ndi akuru a anthu, ku bwalo la mkuru wa ansembe, dzina lace Kayafa;

4. nakhala upo wakuti amgwire Yesu ndi cinyengo, namuphe.

5. Koma ananena iwo, Pa dzuwa la cakudya iai, kuti pasakhale phokoso la anthu.

6. Ndipo pamene Yesu anali m'Betaniya, m'nyumba ya Simoni wakhate,

7. anadza kwa Iye mkazi, anali nayo nsupa yaalabastero ndi mafuta onunkhira bwino a mtengo wapatari, nawatsanulira pamutu pace, m'mene Iye analikukhala pacakudya.

8. Koma m'mene ophunzira anaona, anada mtima, nanena, Cifukwa ninji kuononga kumeneku?

9. Pakuti mafuta awa akadagulitsa ndalama zambiri, ndi kuzipatsa anthu aumphawi.

10. Koma Yesu podziwa, anati kwa iwo, Mumbvutiranji mkaziyu? popeza andicitira Ine nchito yabwino.

11. Pakuti nthawi zonse muli nao aumphawi pamodzi nanu; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

12. Pakuti mkaziyo, m'mene anathira mafuta awa pathupi panga, wandicitiratu ici pa kuikidwa kwanga.

13. Indetu ndinena kwa inu, kumene kuli konse uthenga uwu wabwino udzalalikidwa m'dziko lonse lapansi, ici cimene mkaziyo anacitaci cidzakambidwanso cikumbukiro cace.

14. Pomwepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo, dzina lace Yudase Isikariote, anamuka kwa ansembe akuru,

15. nati, Mufuna kundipatsa ciani, ndipo ine ndidzampereka Iye kwa inu? Ndipo iwo anamwerengera iye ndalama zasiliva makumi atatu.

16. Ndipo kuyambira pamenepo iye anafunafuna nthawi yabwino yakuti ampereke Iye.

Mateyu 26