17. Cimodzimodzinso uyo wa ziwirizo, anapindulapo zina ziwiri.
18. Koma uyo amene analandira imodziyo anamuka, nakumba pansi, naibisa ndalama ya mbuye wace.
19. Ndipo Itapita nthawi yaikuru, anabwera mbuye wa akapolo awo, nawerengera nao pamodzi.
20. Ndipo uyo amene adalandira ndalama za matalente zisanu anadza, ali nazo ndalama zina zisanu, nanena, Mbuye, munandipatsa ndalama za matalente, zisanu, onani ndapindulapo ndalama zisanu zina.