1. Pomwepo Ufumu wa Kumwamba udzafanizidwa ndi anamwali khumi, amene anatenga nyali zao, naturuka kukakomana ndi mkwati.
2. Ndipo asanu a iwo anali opusa, ndi asanu anali ocenjera.
3. Pakuti opusawo, m'mene anatenga nyali zao, sanadzitengeranso mafuta;
4. koma anzeruwo anatenga mafuta m'nsupa zao, pamodzi ndi nyali zao.
5. Ndipo pamene mkwati anacedwa, onsewo anaodzera, nagona tulo.