8. Koma ndizo zonsezi zowawa zoyamba.
9. Pamenepo adzakuperekani kunsautso, nadzakuphani; ndipo anthu a mitundu yonse adzadana nanu, cifukwa ca dzina langa.
10. Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzace, nadzadana wina ndi mnzace.
11. Ndipo aneneri onama ambiri adzauka, nadzasokeretsaanthuambiri.
12. Ndipo cifukwa ca kucuruka kwa kusayeruzika, cikondano ca anthu aunyinji cidzazirala.