Mateyu 24:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. cifukwa Akristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikuru ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

25. Cifukwa cace akanena kwa inu, Onani, Iye ali m'cipululu; musamukeko.

26. Onani, ali m'zipinda; musabvomereze.

27. Pakuti monga mphezi idzera kum'mawa, nionekera kufikira kumadzulo; kotero kudzakhalanso kufika kwace kwa Mwana wa munthu.

Mateyu 24