21. pakuti pomwepo padzakhala masauko akuru, monga sipadakhale otero kuyambira ciyambi ca dziko, kufikira tsopano, inde ndipo sipadzakhalanso.
22. Ndipo akadaleka kufupikitsidwa masiku awo, sakadapulumuka munthu ali yense: koma cifukwa ca osankhidwawo masiku awo adzafupikitsidwa.
23. Pomwepo munthu akanena kwa inu, Onani, Kristu ali kuno, kapena uko musambvomereze;
24. cifukwa Akristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikuru ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.
25. Cifukwa cace akanena kwa inu, Onani, Iye ali m'cipululu; musamukeko.
26. Onani, ali m'zipinda; musabvomereze.