Mateyu 24:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. pakuti pomwepo padzakhala masauko akuru, monga sipadakhale otero kuyambira ciyambi ca dziko, kufikira tsopano, inde ndipo sipadzakhalanso.

22. Ndipo akadaleka kufupikitsidwa masiku awo, sakadapulumuka munthu ali yense: koma cifukwa ca osankhidwawo masiku awo adzafupikitsidwa.

23. Pomwepo munthu akanena kwa inu, Onani, Kristu ali kuno, kapena uko musambvomereze;

24. cifukwa Akristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikuru ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

25. Cifukwa cace akanena kwa inu, Onani, Iye ali m'cipululu; musamukeko.

26. Onani, ali m'zipinda; musabvomereze.

Mateyu 24