12. Ndipo cifukwa ca kucuruka kwa kusayeruzika, cikondano ca anthu aunyinji cidzazirala.
13. Koma iye wakulimbika cilimbikire kufikira kucimariziro, yemweyo adzapulumuka.
14. Ndipo uthenga uwu wabwino wa Ufumu udzalalikidwa pa dziko lonse lapansi, ukhale mboni kwa anthu h mitundu yonse; ndipo pomwepo cidzafika cimariziro.