31. Koma za kuuka kwa akufa, simunawerenga kodi comwe cinanenedwa kwa inu ndi Mulungu, kuti,
32. Ine ndiri Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?Sali Mulungu wa akufa koma wa amoyo.
33. Ndipo pamene makamu a anthu anamva, anazizwa ndi ciphunzitso cace.
34. Koma Afarisi, pakumva kuti Iye anatontholetsa Asaduki, anasonkhana.
35. Ndipo mmodzi wa iwo, mphunzitsi wa cilamulo, anamfunsa ndi kumuyesa Iye, nati,
36. Mphunzitsi, lamulo lalikuru ndi liti la m'cilamulo?
37. Ndipo Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.
38. Ili ndilo lamulo lalikuru ndi loyamba.
39. Ndipo laciwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.
40. Pa malamulo awa awiri mpokolowekapo cilamulo conse ndi aneneri.
41. Ndipo pamene Afarisi anasonkhana, Yesu anawafunsa,
42. nati, Muganiza bwanji za Kristu? ali mwana wa yani? Iwo ananena kwa Iye, Wa Davide.
43. Iye anati kwa iwo, Ndipo Davide mu Mzimu amchula Iye bwanji Ambuye, nanena,
44. Ambuye ananena kwa Ambuye wanga,Ukhale pa dzanja lamanja langa,Kufikira Ine ndidzaika adani ako pansi pa mapazi ako.
45. Cifukwa cace ngati Davide amchula Iye Ambuye, ali mwana wace bwanji? Ndipo panalibe mmodzi anatha kumyankha mau.
46. Ndipo sanalimbika mtima munthu ali yense kumfunsa kanthu kuyambira tsiku lomwelo.