Mateyu 16:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Afarisi ndi Asaduki anadza, namuyesa, namfunsa Iye awaonetse cizindikiro ca Kumwamba.

2. Koma Iye anayankha, nati kwa iwo, Madzulo munena, Kudzakhala ngwe; popeza thambo liri laceza.

3. Ndipo m'mawa, Lero nkwa mphepo; popeza thambo liri la ceza codera. Mudziwa kuzindikira za pa nkhope ya thambo; koma zizindikiro za nyengo yin o, simungathe kuzindikira.

4. Obadwa oipa ndi acigololo afunafuna cizindikiro; ndipo sadzalandira cizindikiro cina, koma cizindikiro ca Yona. Ndipo Iye anawasiya, nacokapo.

5. Ndipo ophunzira anadza ku tsidya linalo, naiwala kutenga mikate.

6. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Yang'anirani mupewe cotupitsa mkate ca Afarisi ndi Asaduki.

7. Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzace, nati, Sitinatenga mikate.

8. Koma Yesu, m'mene anadziwa, anati, Ha, inu okhulupirira pang'ono, mufunsana cifukwa ninji wina ndi mnzace, kuti simunatenga mikate?

Mateyu 16