Mateyu 16:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Afarisi ndi Asaduki anadza, namuyesa, namfunsa Iye awaonetse cizindikiro ca Kumwamba.

2. Koma Iye anayankha, nati kwa iwo, Madzulo munena, Kudzakhala ngwe; popeza thambo liri laceza.

3. Ndipo m'mawa, Lero nkwa mphepo; popeza thambo liri la ceza codera. Mudziwa kuzindikira za pa nkhope ya thambo; koma zizindikiro za nyengo yin o, simungathe kuzindikira.

4. Obadwa oipa ndi acigololo afunafuna cizindikiro; ndipo sadzalandira cizindikiro cina, koma cizindikiro ca Yona. Ndipo Iye anawasiya, nacokapo.

Mateyu 16