Mateyu 12:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Sadzalimbana, sadzapfuula;Ngakhale mmodzi sadzamva mau ace m'makwalala;

20. Bango lophwanyika sadzalityola,Ndi nyali yofuka sadzaizima,Kufikira Iye adzatumiza ciweruzo cikagonjetse,

21. Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lace.

22. Pomwepo anabwera naye kwa Iye munthu wogwidwa ndi ciwanda, wakhungu ndi wosalankhula; ndipo Iye anamciritsa, kotero kuti wosalankhulayo analankhula, napenya.

23. Ndipo makamu onse a anthu anazizwa, nanena, Uyu si mwana wa Davide kodi?

Mateyu 12