Mateyu 10:34-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. 2 Musalingalire kuti nelidadzera kuponya mtendere pa dziko lapansi; sinelinadzera kuponya mtendere, koma lupanga.

35. 3 Pakuti ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wace, ndi mwana wamkazi ndi amace, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wace:

36. ndipo 4 apabanja ace a munthu adzakhala adani ace.

37. 5 Iye wakukonda atate wace, kapena amace koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wace wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.

38. Ndipo 6 iye amene satenga mtanda wace, natsata pambuyo panga, sayenera Ine.

39. 7 Iye amene apeza moyo wace, adzautaya; ndi iye amene ataya moyo wace, cifukwa ca Ine, adzaupeza.

40. 8 Iye wakulandira inu, andilandira Ine, ndi wakundilandira Ine, amlandira Iye amene ananditumiza Ine.

41. 9 Iye wakulandira mneneri, pa dzina la mneneri, adzalandira mphotho ya mneneri; ndipo wakulandira munthu wolungama, pa dzina la munthu wolungama, adzalandira mphotho ya munthu wolungama.

42. Ndipo 10 amenealiyense adzamwetsa mmodzi wa ang'ono awa cikho cokha ca madzi ozizira, pa dzina la wophunzira, indetu ndinena kwa inu, iye sadzataya mphotho yace.

Mateyu 10