Mateyu 10:32-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Cifukwa cace yense amene adzabvomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzambvomereza iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

33. Koma 1 yense amene adzandikana Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzamkana iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

34. 2 Musalingalire kuti nelidadzera kuponya mtendere pa dziko lapansi; sinelinadzera kuponya mtendere, koma lupanga.

35. 3 Pakuti ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wace, ndi mwana wamkazi ndi amace, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wace:

36. ndipo 4 apabanja ace a munthu adzakhala adani ace.

37. 5 Iye wakukonda atate wace, kapena amace koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wace wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.

38. Ndipo 6 iye amene satenga mtanda wace, natsata pambuyo panga, sayenera Ine.

39. 7 Iye amene apeza moyo wace, adzautaya; ndi iye amene ataya moyo wace, cifukwa ca Ine, adzaupeza.

40. 8 Iye wakulandira inu, andilandira Ine, ndi wakundilandira Ine, amlandira Iye amene ananditumiza Ine.

Mateyu 10