30. komatu inu, matsitsi onse a m'mutu mwanu awerengedwa.
31. Cifukwa cace musamaopa; inu mupambana mpheta zambiri.
32. Cifukwa cace yense amene adzabvomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzambvomereza iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.
33. Koma 1 yense amene adzandikana Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzamkana iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.
34. 2 Musalingalire kuti nelidadzera kuponya mtendere pa dziko lapansi; sinelinadzera kuponya mtendere, koma lupanga.
35. 3 Pakuti ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wace, ndi mwana wamkazi ndi amace, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wace: