Masalmo 84:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Apita mwamphamvu naonjezapo mphamvu,Aoneka pamaso pa Mulungu m'Ziyoni.

8. Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa:Cherani khutu, Mulungu wa Yakobo.

9. Onani, Mulungu, ndinu cikopa cathu;Ndipo penyani pa nkhope ya Wodzozedwa wanu.

10. Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena,Kukhala inewapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga,Kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a coipa,

Masalmo 84