Masalmo 37:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7. Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

Masalmo 37