Masalmo 35:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Akhale monga mungu kumphepo,Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6. Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7. Pakuti anandichera ukonde wao m'mbunamo kopanda cifukwa,Anakumbira moyo wanga dzenje kopanda cifukwa.

8. Cimgwere modzidzimutsa cionongeko;Ndipo ukonde wace umene anaucha umkole yekha mwini:Agwemo, naonongeke m'mwemo.

9. Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova:Udzasekera mwa cipulumutso cace.

Masalmo 35