Masalmo 22:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pakuti andizinga agaru:Msonkhano wa oipa wanditsekereza;Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

17. Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:

18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,

19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20. Landitsani moyo wanga kulupanga;Wokondedwa wanga ku mphamvu ya garu,

21. Ndipulumutseni m'kamwa mwa mkango;Inde mwandiyankha ine ndiri pa nyanga za njati,

Masalmo 22