1. Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?
2. Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza;Ndipo usiku, sindikhala cete.
3. Koma Inu ndinu woyera,Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.