6. Nditambalitsira manja anga kwa Inu:Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.
7. Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.Musandibisire nkhope yanu;Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.
8. Mundimvetse cifundo canu mamawa;Popeza ndikhulupirira Inu:Mundidziwitse njira ndiyendemo;Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.
9. Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;Ndibisala mwa Inu.