Masalmo 143:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Nditambalitsira manja anga kwa Inu:Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7. Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.Musandibisire nkhope yanu;Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8. Mundimvetse cifundo canu mamawa;Popeza ndikhulupirira Inu:Mundidziwitse njira ndiyendemo;Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9. Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;Ndibisala mwa Inu.

Masalmo 143