Masalmo 104:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace:Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.

14. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;

15. Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace,Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

16. Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi;Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;

17. M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,

18. Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.

19. Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.

20. Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.

21. Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao,Nifuna cakudya cao kwa Mulungu.

Masalmo 104