Masalmo 102:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.

24. Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.

25. Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.

26. Zidzatha izi, koma Inu mukhala:Inde, zidzatha zonse ngati cabvala;Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:

27. Koma Inu ndinu yemweyo,Ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28. Ana a atumiki anu adzakhalitsa,Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

Masalmo 102