13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.
14. Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yace,Nacitira cifundo pfumbi lace.
15. Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;