32. Ndipo mauwo ananena poyera. Ndipo Petro anamtenga Iye, nayamba kumdzudzula.
33. Koma Iye anapotoloka, napenya ophunzira ace, namdzudzula Petro, nanena, Coka, pita kumbuyo kwanga, Satana iwe; popeza susamalira zinthu za Mulungu, koma za anthu.
34. Ndipo anadziitanira khamulo la anthu pamodzi ndi ophunzira ace, nati kwa iwo, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace, nanditsate Ine.
35. Pakuti yense wakufuna kupulumutsa moyo wace adzautaya; ndipo yense wakutaya moyo wace cifukwa ca Ine, ndi cifukwa ca Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.