9. Cifukwa cace cimene Mulungu anacimanga pamodzi, asacilekanitse munthu.
10. Ndipo m'nyumba ophunzira anamfunsanso za cinthu ici.
11. Ndipo Iye ananena nao, Munthu ali yense akacotsa mkazi wace, nakakwatira wina, acita cigololo kulakwira mkaziyo;
12. ndipo ngati mkazi akacotsa mwamuna wace, nakwatiwa ndi wina, acita cigololo iyeyu.