Maliro 4:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwilo lao,Anatithamangitsa pamapiri natilalira m'cipululu.

20. Wodzozedwa wa Yehova, ndiye mpweya wa m'mphuno mwathu, anagwidwa m'maenje ao; Amene tinanena kuti, Tidzakhala m'mthunzi mwace pakati pa amitundu,

21. Kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu, wokhala m'dzikola Uzi;Cikho cidzapita ngakhale mwa iwenso; udzaledzera ndi kubvulazako.

22. Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni, Yehova sadzakutenganso ndende;Koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu, nadzabvumbulutsa zocimwa zako.

Maliro 4