Maliro 3:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Watsekereza njira zanga ndi miya la yosema, nakhotetsa mayendedwe anga.

10. Andikhalira cirombo colalira kapena mkango mobisalira.

11. Wapambutsa njira zanga, nanding'amba; nandipululutsa.

12. Wathifula uta wace, nandiyesa polozetsa mubvi.

13. Walowetsa m'imso mwanga mibvi ya m'phodo mwace.

Maliro 3