9. Watsekereza njira zanga ndi miya la yosema, nakhotetsa mayendedwe anga.
10. Andikhalira cirombo colalira kapena mkango mobisalira.
11. Wapambutsa njira zanga, nanding'amba; nandipululutsa.
12. Wathifula uta wace, nandiyesa polozetsa mubvi.
13. Walowetsa m'imso mwanga mibvi ya m'phodo mwace.