Maliro 3:49-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Diso langa lingotsanulira osaleka, osapumula,

50. Kufikira Yehova adzazolika kumwamba ndi kuona;

51. Diso langa limvetsa moyo wanga zowawa cifukwa ca ana akazi onse a m'mudzi mwanga.

52. Ondida opanda cifukwa anandiinga ngati mbalame;

53. Anaononga moyo wanga m'dzenje, naponya mwala pamwambapaine;

54. Madzi anayenda pamwamba pa mutu panga, ndinati, dalikhidwa.

55. Ndinaitana dzina lanu, Yehova, ndiri m'dzenje lapansi;

56. Munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi popfuulaine.

57. Munayandikira tsiku la kukuitanani ine; munati, Usaope.

Maliro 3