22. Cifukwa cakusathedwa ife ndico cifundo ca Yehova, pakuti cisoni cace sicileka;
23. Cioneka catsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.
24. Moyo wanga uti, Gawo langa ndiye Yehova; cifukwa cace ndidzakhulupirira.
25. Yehova akhalira wabwino omlindirira, ndi moyo womfunafuna.
26. Nkokoma kuti munthu ayembekeze ndi kulindirira modekha cipulumutso ca Yehova.
27. Nkokoma kuti munthu asenze gori ali wamng'ono.