Maliro 3:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Watarikitsanso moyo wanga ndi mtendere; ndinaiwala zabwino.

18. Ndipo ndinati, Mphamvu yanga yatha, osayembekezanso kanthu kwa Yehova.

19. Kumbukirani msauko Wanga ndi kusocera kwanga, ndizo civumulo ndi ndulu.

20. Moyo wanga uzikumbukirabe nuwerama mwa ine,

21. Ndiri naco ciyembekezo popeza ndilingalira ici ndiyembekeza kanthu.

22. Cifukwa cakusathedwa ife ndico cifundo ca Yehova, pakuti cisoni cace sicileka;

Maliro 3