3. Koma pamene Paulo adaola cisakata ca nkhuni, naciika pamoto, inaturukamo njoka, cifukwa ca kutenthaku, nilumadzanja lace.
4. Koma pamene akunjawo anaona ciromboco ciri lende pa dzanja lace, ananena wina ndi mnzace, Zoona munthuyu ndiye wambanda, angakhale anapulumuka m'nyanja, cilungamo sicimlola akhale ndi moyo.
5. Koma anakutumulira ciromboco kumoto, osamva kupweteka.