Macitidwe 19:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Onsewo anali ngati amuna khumi ndi awiri.

8. Ndipo iye analowa m'sunagoge, nanena molimba mtima, miyezi itatu, natsutsana ndi kukopa kunena za Ufumu wa Mulungu.

9. Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo pamaso pa anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse m'sukulu ya Turano.

10. Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene.

Macitidwe 19