Macitidwe 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali pa Ikoniyo kuti analowa pamodzi m'sunagoge wa Ayuda, nalankhula kotero, kuti khamu lalikuru la Ayuda ndi Ahelene anakhulupira.

2. Koma Ayuda osamvefa anautsa mitima ya Ahelene kuti aipse abale athu.

3. Cifukwa cace anakhala nthawi yaikuru nanenetsa zolimba mtima mwa Ambuye, amene anacitira umboni mau a cisomo cace, napatsa zizindikiro ndi zozizwa kuti zicitidwe ndi manja ao.

4. Ndipo khamu la mudziwo linagawikana; ena analindi Ayuda, komaena anali ndi atumwi.

Macitidwe 14