Macitidwe 10:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo panali pakulowa Petro, Komeliyo anakomana naye, nagwa pa mapazi ace, namlambira.

26. Koma Petro anamuutsa iye, nanena, Nyamuka; inenso ndine munthu.

27. Ndipo pakukamba naye, analowa, napeza ambiri atasonkhana;

28. ndipo anati kwa iwo, Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina; koma Mulungu anandionetsera ine ndisanenere ali yense ali munthu wamba kapena wonyansa;

29. cifukwa cacenso ndinadza wosakana, m'mene munatuma kundiitana. Pamenepo ndifunsa, mwandiitaniranji?

Macitidwe 10