Luka 8:42-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. cifukwa anali naye mwana wamkazi mmodzi yekha, wa zaka zace ngati khumi ndi ziwiri, ndipo analinkumwalira iye, Koma pakupita iye anthu a mipingo anakanikizana naye,

43. Ndipo mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, amene adasudzula asing'anga za moyo wace zonse, ndipo sanathe kuciritsidwa ndi mmodzi yense,

44. anadza pambuyo pace, nakhudza mphonje yacobvala cace; ndipo pomwepo nthenda yace inaleka.

45. Ndipo Yesu anati, Wandikhudza Ine ndani? Koma pamene onse anakana, Petro ndi iwo akukhala naye anati, Ambuye, anthu aunyinji alikukankhana pa Inu ndi kukanikizana.

Luka 8