13. Ndipo iye anatambalitsa dzanja lace, namkhudza, nanena, Ndifuna, takonzeka, Ndipo pomwepo khate linacoka kwa iye.
14. Ndipo iye anamuuzitsa, kuti asanene kwa munthu ali yense; koma ucoke, nudzionetse wekha kwa wansembe, nupereke nsembe ya pa cikonzedwe cako, monga adalamulira Mose, kukhale umboni kwa iwo.
15. Koma makamaka mbiri yace ya iye inabuka: ndipo mipingo yambiri ya anthu inasonkhanakudzamvera, ndi kudzaciritsidwa nthenda zao.
16. Koma iye anazemba, nanka m'mapululu, nalikupemphera.
17. Ndipo panali tsiku limodzi la masiku awo, iye analikuphunzitsa; ndipo analikukhalapo Afarisi ndi aphunzitsi a malamulo, amene anacokera ku midzi yonse ya ku Galileya, ndi Yudeya ndi Yerusalemu: ndipo mphamvu ya Ambuye inali ndi iye yakuwaciritsa,