3. Ndipo iye anadza ku dziko lonse la m'mbali mwa Yordano, nalalikira ubatizo wa kulapa mtima kuloza ku cikhululukiro ca macimo;
4. monga mwalembedwa m'kalata wa mau a Yesaya mneneri, kuti,Mau a wopfuula m'cipululu,Konzani khwalala la Ambuye,Lungamitsani njira zace.
5. Cigwa ciri conse cidzadzazidwa,Ndipo phiri liri lonse ndi mtunda uti wonse zidzacepsedwa;Ndipo zokhota zidzakhala zolungama,Ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala;
6. Ndipo anthu onse adzaona cipulumutso ca Mulungu.
7. Cifukwa cace iye ananena kwa makamuwo a anthu amene anaturukira kukabatizidwa ndi iye, Obadwa a njoka inu, anakulangizani inu ndani kuthawa mkwiyo ulinkudza?
8. Cifukwa cace balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.