Luka 12:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo anati, Ndidzatere: ndidzapasula nkhokwe zanga, ndi kumanganso zazikuru, ndipo ndidzasungiramo dzinthu zanga zonse, ndi cuma canga.

19. Ndipo ndidzati kwa moyo wanga, Moyo iwe, uli naco cuma cambiri cosungika kufikira zaka zambiri; tapumulatu, nudye, numwe, nukondwere.

20. Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?

21. Atero iye wakudziunjikira cuma mwini yekha wosakhala naco cuma ca kwa Mulungu,

Luka 12