22. koma pamene pali ponse amdzera wakumposa mphamvu, nakamlaka, amcotsera zida zace zonse zimene anazitama, nagawa zofunkha zace.
23. Iye wosabvomerezana ndi Ine atsutsana ndi Ine; ndipo iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwaza.
24. Pamene pali ponse mzimu wonyansa ukaturuka mwa munthu, upyola malo opanda madzi nufunafuna mpumulo; ndipo posaupeza unena, Ndidzabwera kunyumba kwanga kumene ndinaturukako;
25. ndipo pofika, uipeza yosesa ndi yokonzeka.
26. Pomwepo, upita nutenga mizimu yina isanu ndi iwiri yoipa yoposa ndi uwu mwini; ndipo ilowa nikhalira komweko; ndipo makhalidwe otsiriza a munthu uyu aipa koposa oyambawo.