Luka 1:38-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Ndipo Mariya anati, Onani, mdzakazi wa Ambuye; kukhale kwa ine monga mwa mau anu. Ndipo mngelo anacoka kwa iye.

39. Ndipo Mariya ananyamuka masiku amenewa, namuka ndi cangu ku dziko la mapiri ku mudzi wa Yuda;

40. nalowa m'nyumba ya Zakariya, nalankhula Elisabeti.

41. Ndipo panali pamene Elisabeti anamva kulankhula kwace kwa Mariya, mwana wosabadwayo anatsalima m'mimba mwace; ndipo Elisabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera;

42. nakweza mau ndi mpfuu waukuru, nati, 2 Wodalitsika iwe mwa akazi, ndipo codalitsika cipatso ca mimba yako,

43. Ndipo ici cicokera kuti kudza kwa ine, kuti adze kwa ine amace wa Ambuye wanga?

Luka 1