Luka 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. POPEZA ambiri anayesa kulongosola nkhani ya zinthu zinacitika pakati pa ife,

2. monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,

3. kuyambira paciyambi, ndinayesa nkokoma inenso, amene ndinalondalonda mosamalitsa zinthu zonse kuyambira paciyambi, kulembera kwa iwe tsatane tsatane, Teofilo wabwinotu iwe;

4. kuti udziwitse zoona zace za mau amene unaphunzira.

Luka 1