Levitiko 9:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo anati kwa Aroni, Dzitengere mwana wa ng'ombe wamwamuna, akhale nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo ikhale nsembe yopsereza, zopanda cirema, nubwere nazo pamaso pa Yehova.

3. Nunene kwa ana a Israyeli, ndi kuti, Dzitengereni tonde akhale nsembe yaucimo; ndi mwana wa ng'ombe, ndi mwana wa nkhosa, a caka cimodzi, opanda cirema, akhale nsembe yopsereza;

4. ndi ng'ombe, ndi nkhosa yamphongo zikhale zakuyamika, kuziphera nsembe pamaso pa Yehova; ndi nsembe yaufa yosanganiza ndi mafuta; pakuti lero Yehova wakuonekerani inu.

5. Pamenepo anatenga zimene Mose anawauza, napita nazo pakhomo pa cihema cokomanako; ndi msonkhano wonse unasendera kufupi nuimirira pamaso pa Yehova,

Levitiko 9