44. Ndiponso pali icinso: pokhala iwo m'dziko la adani ao sindidzawakaniza, kapena kunyansidwa nao, kuwaononga konse, ndi kutyola pangano langa ndinapangana nao; popeza Ine ndine Yehova Muhmgu wao.
45. Koma cifukwa ca iwo ndidzawakumbukila pangano la makolo ao, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto pamaso pa amitundu, kuti ndikhale Mulungu wao; Ine ndine Yehova.
46. Awa ndi malemba ndi maweruzo ndi malamulo amene Yehova anaika pakati pa iye ndi ana a Israyeli m'phiri la Sinai, ndi dzanja la Mose.