1. Musamadzipangira mafano, kapena kudziutsira mafano osema, kapena coimiritsa, kapena kuika mwala wozokota m'dziko mwanu kuugwadira umene; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
2. Musunge masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
3. Mukamayenda m'malemba anga, ndi kusunga malamulo anga, ndi kuwacita;