11. Muciyese caka ca makomi asanuco coliza lipenga, musamabzala, kapena kuceka zophuka zokha m'mwemo; kapenakuceka mphesa zace za mipesa yosadzombola.
12. Popeza ndico caka coliza lipenga; muciyese copatulika, mudye zipatso zace kunja kwa munda.
13. Caka coliza lipenga ici mubwerere nonse ku zace zace.
14. Ndipo ukagulitsa kanthu kwa mnansi wako, kapena kugula kanthu ka mnansi wako, musamasautsana;